MPHEKESERA ZOWAMANGA A MONIKA CHAKWERA ZICHOSETSA NTCHITO A CHIZUMA
Mkulu wa nthambi ya Anti-Corruption Bureau (ACB) a Martha Chizuma asanachotsedwe ntchito, mtsogoleri wa dziko lino a Lazarus Chakwera anali atamva mphekesera zomwe zimanena kuti nthambi ya ACB ikufuna kumanga akazi awo, a Monika Chakwera ndipo izi zinawatutumusa. A Chakwera anamva nkhani imeneyi kuchokera kwa munthu wina wamkulu wogwira ntchito m’boma ndipo mphekeserazi zimanenanso kuti mwana wamkulu wa a Chakwera, Nick amangidwanso limodzi ndi mayi ake pomuganizira kuti akuchita zinthu za katangale komanso ziphuphu. Izi zinadza pamene zikumnvekanso kuti nthambi ya ACB inali ikumaliza kafukufuku wake wokhudza kuphwanya malamulo pa ntchito kwa mlembi wa mtsogoleri ndi nduna a Colleen Zamba komanso mkulu wakale woyimira boma pa milandu a Steve Kayuni.
7 авг 2024